119 | GEN 5:13 | Atabadwa Mahalaleli, Kenani anakhala ndi moyo zaka zina 840 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. |
153 | GEN 6:15 | Uchipange motere: Chombo chikhale mamita 140 mulitali, mamita 23 mulifupi ndi mamita 13 mu msinkhu wake. |
280 | GEN 11:13 | Atabereka Sela, Aripakisadi anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi. |
282 | GEN 11:15 | Atabereka Eberi, Sela anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi. |
283 | GEN 11:16 | Pamene Eberi anali ndi zaka 34 anabereka Pelegi. |
284 | GEN 11:17 | Atabereka Pelegi, Eberi anakhala ndi moyo zaka zina 430 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi. |
374 | GEN 15:13 | Tsono Yehova anati kwa iye, “Uyenera kudziwa mosakayika kuti zidzukulu zako zidzakhala alendo mʼdziko lachilendo ndipo zidzakhala akapolo ndi kuzunzidwa zaka 400. |
453 | GEN 18:28 | bwanji anthu olungama atacheperapo ndi asanu pa anthu makumi asanu? Kodi mudzawononga mzinda wonse chifukwa cha asanuwo?” Iye anati, “Nditapezamo anthu 45, sindidzawuwononga.” |
454 | GEN 18:29 | Kenakanso anayankhula kwa Iye nati, “Bwanji atangopezekamo anthu 40 okha?” Iye anayankha, “Chifukwa cha anthu 40 amenewa, sindidzatero.” |
587 | GEN 23:15 | “Mundimvere mbuye wanga; mundawo mtengo wake ndi masekeli asiliva okwana 400. Koma zimenezo nʼchiyani pakati pa ine ndi inu? Ikani mtembo wa mkazi wanu.” |
588 | GEN 23:16 | Abrahamu anavomera mtengo umene ananena Efroni Ahiti onse akumva ndipo anamuwerengera masekeli asiliva okwana 400 monga mwa mtengo wa ndalama umene amalonda a nthawi imeneyo ankagwiritsa ntchito. |
727 | GEN 26:34 | Pamene Esau anali ndi zaka 40, anakwatira Yuditi mwana wamkazi wa Beeri Mhiti. Anakwatiranso Basemati mwana wa mkazi wa Eloni Mhiti. |
935 | GEN 32:7 | Pamene amithenga aja anabwerera kwa Yakobo, anati, “Tinapita kwa mʼbale wanu Esau, ndipo tsopano iye akubwera kudzakumana nanu. Ali ndi anthu 400.” |
944 | GEN 32:16 | ngamira za mkaka 30 ndi ana awo, ngʼombe zazikazi 40 ndi zazimuna khumi, ndipo abulu aakazi makumi awiri ndi abulu aamuna khumi. |
962 | GEN 33:1 | Yakobo atakweza maso ake anaona Esau akubwera ndi anthu ake 400. Choncho ana ake anawagawira Leya, Rakele ndi antchito awiri aja. |
1449 | GEN 47:28 | Yakobo anakhala ku Igupto zaka 17 ndipo zaka za moyo wake zinali 147. |
1510 | GEN 50:3 | Antchito aja zinawatengera masiku 40 kuti akonze mtembo uja popeza ntchito ngati imeneyi inafunikira masiku monga amenewa. Ndipo Aigupto anamulira Yakobo kwa masiku makumi asanu ndi awiri. |
1835 | EXO 12:18 | Mwezi woyamba muzidzadya buledi wopanda yisiti kuyambira madzulo tsiku la 14 la mweziwo mpaka tsiku la 21 mwezi womwewo. |
1857 | EXO 12:40 | Ndipo Aisraeli anakhala ku Igupto kwa zaka 430. |
1858 | EXO 12:41 | Pa tsiku lomwelo limene anakwanitsa zaka 430, magulu onse a Yehova anatuluka mʼdziko la Igupto. |
1983 | EXO 16:35 | Aisraeli anadya mana zaka 40, mpaka pamene anafika ku dziko kumene amati akakhazikeko. Iwo anadya mana mpaka pamene anafika mʼmalire a Kanaani. |
2196 | EXO 24:18 | Ndipo Mose analowa mʼmitambo nakwera phiri. Iye anakhala ku phiriko 40 usana ndi usiku. |
2206 | EXO 25:10 | “Tsono apange bokosi lamatabwa amtengo wa mkesha, ndipo kutalika kwake kukhale masentimita 114, mulifupi mwake masentimita 69, msinkhu wake masentimita 69. |
2213 | EXO 25:17 | “Upange chivundikiro cha bokosilo cha golide wabwino kwambiri, kutalika kwake masentimita 114, mulifupi mwake masentimita 69. |
2219 | EXO 25:23 | “Upange tebulo la matabwa amtengo wa mkesha, mulitali mwake masentimita 91, mulifupi mwake masentimita 46, msinkhu wake masentimita 69. |
2235 | EXO 25:39 | Choyikapo nyale ndi zipangizo zonse zipangidwe ndi golide wabwino kwambiri wolemera makilogalamu 34. |
2249 | EXO 26:13 | Nsalu yotsalira ya masentimita 46 mulitali mwake mʼmbali zonse ziwiri idzalendewere kuphimba mbali ziwirizo. |
2255 | EXO 26:19 | Ndipo upange matsinde 40 asiliva ndipo uwayike pansi pa maferemuwo. Pansi pa feremu iliyonse pakhale matsinde awiri ogwiriziza zolumikizira ziwiri zija. |
2257 | EXO 26:21 | Upangenso matsinde 40 asiliva, awiri pansi pa feremu iliyonse. |
2282 | EXO 27:9 | “Upange bwalo la chihema. Mbali yakummwera ikhale yotalika mamita 46 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga yofewa yosalala yolukidwa bwino. |
2284 | EXO 27:11 | Mbali yakumpoto ikhalenso yotalika mamita 46 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga. Pakhalenso mizati makumi awiri, matsinde amkuwa makumi awiri, ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo. |
2291 | EXO 27:18 | Kutalika kwa bwalolo kukhale mamita 46, mulifupi mwake mamita 23, msinkhu wake masentimita 230. Nsalu ya katani ikhale yofewa ndi yosalala bwino. Matsinde ake akhale amkuwa. |
2385 | EXO 30:2 | Likhale lofanana mbali zonse. Mulitali masentimita 46, mulifupi masentimita 46, ndipo msinkhu masentimita 91. Nyanga zake zipangidwe kumodzi ndi guwalo. |
2525 | EXO 34:28 | Mose anakhala kumeneko pamodzi ndi Yehova masiku 40, usana ndi usiku, wosadya kanthu kapena kumwa madzi. Ndipo iye analemba pa miyala ija mawu a pangano, malamulo khumi. |
2591 | EXO 36:24 | ndiponso anapanga matsinde 40 asiliva ndipo anawayika pansi pa maferemuwo. Pansi pa feremu iliyonse anayika matsinde awiri ogwiriziza zolumikizira ziwiri zija. |
2606 | EXO 37:1 | Bezaleli anapanga Bokosi la Chipangano lamatabwa amtengo wa mkesha. Kutalika kwake kunali masentimita 114, mulifupi mwake munali masentimita 69, msinkhu wake masentimita 69. |
2611 | EXO 37:6 | Iye anapanga chivundikiro cha bokosilo cha golide wabwino kwambiri, kutalika kwake masentimita 114, mulifupi mwake masentimita 69. |
2615 | EXO 37:10 | Iwo anapanga tebulo la matabwa amtengo wa mkesha, mulitali mwake masentimita 91, mulifupi mwake masentimita 46, msinkhu wake masentimita 69. |
2629 | EXO 37:24 | Iwo anapanga choyikapo nyale ndi zipangizo zake zonse zagolide wabwino kwambiri wolemera makilogalamu 34. |
2630 | EXO 37:25 | Iwo anapanga guwa lamatabwa amtengo wa mkesha lofukizirapo lubani. Linali lofanana mbali zonse, mulitali masentimita 46, mulifupi masentimita 46, ndipo msinkhu masentimita 91, ndipo nyanga zake zinapangidwa kumodzi ndi guwalo. |
2643 | EXO 38:9 | Kenaka anapanga bwalo la chihema. Mbali yakummwera inali yotalika mamita 46 ndipo kunali nsalu yotchinga yofewa yosalala yolukidwa bwino. |
2645 | EXO 38:11 | Mbali yakumpoto inalinso yotalika mamita 46 ndipo inali ndi mizati makumi awiri, matsinde amkuwa makumi awiri, ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo. |
2659 | EXO 38:25 | Siliva wochokera ku gulu lonse la anthu anali wolemerera makilogalamu 3,430, potsata miyeso ya ku malo wopatulika. |
2661 | EXO 38:27 | Anagwiritsa ntchito siliva wolemera makilogalamu 3,400 kupanga matsinde 100 a ku malo wopatulika ndi makatani, ndipo makilogalamu 34 kupanga tsinde limodzi. |
2663 | EXO 38:29 | Mkuwa ochokera ku nsembe yoweyula unali makilogalamu 2,425. |
3408 | LEV 23:5 | Chikondwerero cha Paska chiziyamba madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba. |
3478 | LEV 25:8 | “ ‘Muzichotsera Masabata asanu ndi awiri a zaka, ndi kuchulukitsa zaka zisanu ndi ziwiri kasanu ndi kawirinso kuti Masabata asanu ndi awiri a zakawo akwane zaka 49. |
3626 | NUM 1:21 | Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500. |
3630 | NUM 1:25 | Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650. |
3632 | NUM 1:27 | Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600. |
3634 | NUM 1:29 | Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400. |
3636 | NUM 1:31 | Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400. |
3638 | NUM 1:33 | Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500. |
3642 | NUM 1:37 | Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400. |
3646 | NUM 1:41 | Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500. |
3648 | NUM 1:43 | Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400. |
3663 | NUM 2:4 | Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 74,600. |
3665 | NUM 2:6 | Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 54,400. |
3667 | NUM 2:8 | Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 57,400. |
3668 | NUM 2:9 | Anthu onse aamuna mʼmisasa ya Yuda, chiwerengero chawo ndi 186,400 monga mwa magulu awo. Iwowo ndiwo aziyamba kusamuka. |
3670 | NUM 2:11 | Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 46,500. |
3674 | NUM 2:15 | Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 45,650. |
3675 | NUM 2:16 | Anthu onse aamuna mu msasa wa Rubeni, chiwerengero chawo monga mwa magulu awo, ndi 151,450. Iwowo azikhala achiwiri posamuka. |
3678 | NUM 2:19 | Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 40,500. |
3682 | NUM 2:23 | Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 35,400. |
3687 | NUM 2:28 | Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 41,500. |
3689 | NUM 2:30 | Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 53,400. |
3939 | NUM 7:88 | Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yachiyanjano chinali motere: ngʼombe zothena 24, nkhosa zazimuna 60, mbuzi zazimuna 60 ndi ana ankhosa aamuna a chaka chimodzi 60. Zimenezi ndi zimene zinali zopereka zopatulira guwa lansembe litadzozedwa. |
3964 | NUM 8:24 | “Ntchito za Alevi ndi izi: Amuna a zaka 24 kapena kuposera pamenepa ndiye azibwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano. |
3969 | NUM 9:3 | Muzichita Paska pa nthawi yake yoyikika, madzulo a tsiku la 14 la mwezi uno, potsata malamulo ndi malangizo ake.” |
3971 | NUM 9:5 | ndipo anachitadi Paskayo mʼchipululu cha Sinai madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba. Aisraeli anachita zonse monga momwe Yehova analamulira Mose. |
3977 | NUM 9:11 | Azichita chikondwererochi madzulo a pa tsiku la 14 la mwezi wachiwiri. Azidya mwana wankhosa wamwamuna pamodzi ndi buledi wopanda yisiti ndi ndiwo zowawa zamasamba. |
4244 | NUM 17:14 | Komabe anthu 14, 700 anafa ndi mliriwo, kuwonjezera pa aja amene anafa chifukwa cha Kora. |
4481 | NUM 25:9 | Pa mliriwo, anthu okwana 24,000 anafa. |
4498 | NUM 26:7 | Awa anali mafuko a Rubeni: onse amene anawerengedwa analipo 43,730. |
4509 | NUM 26:18 | Awa ndiwo anali mafuko a Gadi. Onse amene anawerengedwa analipo 40,500. |
4516 | NUM 26:25 | Awa ndi amene anali a fuko la Isakara. Amene anawerengedwa analipo 64,300. |
4532 | NUM 26:41 | Awa ndiwo anali mabanja a Benjamini. Amene nawerengedwa analipo 45,600. |
4534 | NUM 26:43 | Onse a fuko la Asuhamu amene anawerengedwa analipo 64,400. |
4538 | NUM 26:47 | Awa ndiwo anali mafuko a Aseri. Onse amene anawerengedwa analipo 53,400. |
4541 | NUM 26:50 | Awa ndiwo anali mafuko a Nafutali. Onse amene anawerengedwa analipo 45,400. |
4595 | NUM 28:16 | “ ‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita Paska wa Yehova. |
4851 | NUM 35:4 | “Malo a msipu a mudziwo amene mudzawapatse Aleviwo, adzayambire ku khoma la mudzi ndipo adzatuluke kunja mamita 450, kuzungulira mudziwo. |
4853 | NUM 35:6 | “Isanu ndi umodzi mwa midzi imene mudzapereke kwa Alevi idzakhala mizinda yopulumukirako, kumene munthu wopha mnzake adzathawireko. Ndipo mudzawapatsenso midzi ina 42. |
4854 | NUM 35:7 | Midzi yonse imene mudzapereke kwa Alevi idzakhale 48, pamodzi ndi malo oweterako ziweto. |
5925 | JOS 4:13 | Asilikali pafupifupi 40,000 anawoloka napita kukayima mʼchigwa cha Yeriko kukonzekera nkhondo. |
5946 | JOS 5:10 | Akupumulabe ku Giligala kuja mʼchigwa cha Yeriko, Aisraeli anachita chikondwerero cha Paska madzulo pa tsiku la 14 la mwezi woyamba womwewo. |
6199 | JOS 14:10 | “Tsono papita zaka 45 chiyankhulire Yehova zimenezi kwa Mose. Nthawi imeneyo nʼkuti Aisraeli akuyendayenda mʼchipululu. Yehova wandisunga ndipo tsopano ndili ndi zaka 85. |
6240 | JOS 15:36 | Saaraimu, Aditaimu, ndi Gederi (kapena Gederotaimu). Mizinda yonse inalipo 14 pamodzi ndi midzi yake yozungulira. |
6323 | JOS 18:28 | Zera Haelefu, mzinda wa Ayebusi (ndiye kuti Yerusalemu) Gibeya ndi Kiriati, mizinda 14 ndi midzi yake. Limeneli ndilo dziko limene mabanja a fuko la Benjamini analandira kuti likhale lawo. |
6424 | JOS 21:41 | Motero mizinda 48 ya mʼdziko limene Aisraeli analanda inapatsidwa kwa Alevi, kuphatikizapo malo ake odyetsera ziweto. |
6633 | JDG 5:8 | Pamene anasankha milungu ina, nkhondo inabwera ku zipata za mzinda, ndipo chishango kapena mkondo sizinapezeke pakati pa anthu 40,000 mu Israeli. |
6749 | JDG 8:28 | Choncho Amidiyani anagonjetsedwa ndi Aisraeli ndipo sanayeserenso kuwawukira. Ndipo dzikolo linakhala pa mtendere kwa zaka 40 pamene Gideoni anali ndi moyo. |
6877 | JDG 12:6 | Ndiye amamuwuza kuti, “Nena kuti ‘Shiboleti.’ ” Tsono munthuyo akanena kuti Siboleti popeza samatha kutchula bwino mawuwa, ankamugwira ndi kumupha pomwepo pa madooko a mtsinje wa Yorodani. Nthawi imeneyo anaphedwa Aefereimu 42,000. |
7058 | JDG 20:2 | Atsogoleri a anthu onse ndi a mafuko onse Aisraeli anali nawo pa msonkhano wa anthu a Mulungu. Onse pamodzi analipo asilikali oyenda pansi 400,000 atanyamula malupanga. |