104 | GEN 4:24 | Ngati wopha Kaini amulipsira kasanu nʼkawiri, ndiye kuti wopha ine Lameki adzamulipsira kokwanira 77.” |
113 | GEN 5:7 | Atabadwa Enosi, Seti anakhala ndi moyo zaka zina 807 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. |
118 | GEN 5:12 | Pamene Kenani anali ndi zaka 70, anabereka Mahalaleli. |
131 | GEN 5:25 | Pamene Metusela anali ndi zaka 187, anabereka Lameki. |
132 | GEN 5:26 | Ndipo atabadwa Lameki, Metusela anakhala ndi moyo zaka zina 782 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. |
137 | GEN 5:31 | Zaka zonse za Lameki zinali 777, ndipo kenaka anamwalira. |
171 | GEN 7:11 | Pa tsiku la 17 la mwezi wachiwiri, Nowa ali ndi zaka 600, akasupe onse akuya kwambiri anasefuka ndiponso zitseko za madzi akumwamba zinatsekuka. |
188 | GEN 8:4 | ndipo pa tsiku la 17 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, chombo chija chinakakhazikika pa mapiri a Ararati. |
198 | GEN 8:14 | Pokwana tsiku la 27 la mwezi wachiwiri dziko lapansi linawumiratu. |
288 | GEN 11:21 | Atabereka Serugi, Reu anakhala ndi moyo zaka zina 207 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi. |
293 | GEN 11:26 | Pamene Tera anali ndi zaka 70, anabereka Abramu, Nahori ndi Harani. |
303 | GEN 12:4 | Choncho Abramu ananyamuka monga momwe Yehova anamuwuzira, napita pamodzi ndi Loti. Pamene Abramu amachoka ku Harani nʼkuti ali ndi zaka 75. |
573 | GEN 23:1 | Sara anakhala ndi moyo zaka 127. |
666 | GEN 25:7 | Abrahamu anakhala ndi moyo zaka 175. |
676 | GEN 25:17 | Ismaeli anakhala ndi moyo zaka 137. Iye anamwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake. |
1086 | GEN 37:2 | Mbiri ya banja la Yakobo ndi iyi: Yosefe, mnyamata wa zaka 17 ankaweta nkhosa ndi abale ake, pamodzi ndi ana a Biliha ndi Zilipa, akazi a abambo ake. Tsono Yosefe ankabwera kudzawuza abambo ake zoyipa za abale ake. |
1414 | GEN 46:27 | Pophatikiza ana awiri a Yosefe obadwira ku Igupto, anthu a pa banja la Yakobo amene anapita ku Igupto, onse pamodzi analipo 70. |
1449 | GEN 47:28 | Yakobo anakhala ku Igupto zaka 17 ndipo zaka za moyo wake zinali 147. |
1538 | EXO 1:5 | Anthu onse obadwa mwa Yakobo analipo 70. Yosefe nʼkuti ali kale ku Igupto. |
1672 | EXO 6:16 | Mayina a ana a Levi pamodzi ndi zidzukulu zawo anali awa: Geresoni, Kohati ndi Merari. Levi anakhala ndi moyo kwa zaka 137. |
1676 | EXO 6:20 | Amramu anakwatira Yokobedi mlongo wa abambo ake, amene anabereka Aaroni ndi Mose. Amramu anakhala ndi moyo kwa zaka 137. |
2274 | EXO 27:1 | “Upange guwa lansembe lamatabwa amtengo wa mkesha. Likhale lofanana mbali zonse, msinkhu wake masentimita 137, mulitali mwake masentimita 229, mulifupi mwake masentimita 229. |
2635 | EXO 38:1 | Anapanga guwa lansembe zopsereza lamatabwa amtengo wa mkesha. Linali lofanana mbali zonse. Msinkhu wake masentimita 137, mulitali mwake masentimita 229, mulifupi masentimita 229. |
3632 | NUM 1:27 | Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600. |
3636 | NUM 1:31 | Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400. |
3644 | NUM 1:39 | Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700. |
3663 | NUM 2:4 | Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 74,600. |
3667 | NUM 2:8 | Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 57,400. |
3685 | NUM 2:26 | Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 62,700. |
3690 | NUM 2:31 | Anthu onse aamuna mu msasa wa Dani chiwerengero chawo ndi 157,600. Iwo azidzanyamuka pomaliza, ndi mbendera zawo. |
3715 | NUM 3:22 | Chiwerengero cha amuna onse amene anawawerenga a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 7,500. |
3736 | NUM 3:43 | Chiwerengero chonse cha ana aamuna oyamba kubadwa kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 22, 273. |
3739 | NUM 3:46 | Pofuna kuwombola ana aamuna 273 oyamba kubadwa a Aisraeli amene anaposa chiwerengero cha aamuna a fuko la Levi, |
3780 | NUM 4:36 | atawawerenga mwa mafuko awo, anali 2,750. |
3936 | NUM 7:85 | Mbale iliyonse yasiliva inkalemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndipo beseni lililonse lowazira linkalemera magalamu 800. Pamodzi, mbale zonse zasiliva zinkalemera makilogalamu 27 monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. |
4041 | NUM 11:16 | Yehova anawuza Mose kuti, “Undibweretsere anthu 70 ochokera pakati pa akuluakulu a Aisraeli, amene umawadziwa kuti ndiwo atsogoleri komanso akuluakulu a mabanja. Abwere ku tenti ya msonkhano kuti ayime kumeneko pamodzi ndi iwe. |
4244 | NUM 17:14 | Komabe anthu 14, 700 anafa ndi mliriwo, kuwonjezera pa aja amene anafa chifukwa cha Kora. |
4498 | NUM 26:7 | Awa anali mafuko a Rubeni: onse amene anawerengedwa analipo 43,730. |
4513 | NUM 26:22 | Awa ndiwo anali mafuko a Yuda. Amene anawerenga analipo 76,500. |
4525 | NUM 26:34 | Awa ndiwo anali mafuko a Manase. Amene anawerengedwa analipo 52,700. |
4542 | NUM 26:51 | Chiwerengero chonse cha amuna mu Israeli chinalipo 601,730. |
4698 | NUM 31:32 | Zotsala pa zolanda ku nkhondo zimene ankhondowo anatenga zinali nkhosa 675,000, |
4699 | NUM 31:33 | Ngʼombe 72,000, |
4702 | NUM 31:36 | Gawo la ankhondo amene anapita ku nkhondo linali: nkhosa 337,500, |
4703 | NUM 31:37 | mwa zimenezi gawo la Yehova linali 675; |
4704 | NUM 31:38 | ngʼombe zinalipo 36,000 ndipo gawo la Yehova linali 72; |
4709 | NUM 31:43 | Tsono gawo la Aisraeli linali ili: nkhosa 337,500, |
4771 | NUM 33:9 | Atachoka ku Mara anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe a madzi khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa 70 ndipo anamanga misasa yawo kumeneko. |
6518 | JDG 1:7 | Tsono Adoni-Bezeki anati, “Mafumu 70 omwe anadulidwa zala zazikulu za ku manja ndi miyendo yawo ankatola nyenyeswa pansi pa tebulo langa. Mulungu tsopano wandibwezera zomwe ndinawachita.” Kenaka anapita naye ku Yerusalemu ndipo anafera komweko. |
6735 | JDG 8:14 | Kumeneko iye anagwira mnyamata wa ku Sukoti ndipo atamufunsa, mnyamatayo anamulembera mayina a akuluakulu ndi atsogoleri 77 a ku Sukoti. |
6751 | JDG 8:30 | Ana a Gideoni anali 70 popeza anali ndi akazi ambiri. |
6760 | JDG 9:4 | Tsono anamupatsa ndalama zasiliva 70 za mʼnyumba ya chipembedzo ya Baala Beriti. Ndi ndalama zimenezi Abimeleki analemba anthu achabechabe ndi osasamala kuti azimutsatira. |
6774 | JDG 9:18 | Koma lero inu mwawukira banja la abambo anga. Mwapha ana ake 70 pa mwala umodzi, ndiponso mwalonga ufumu Abimeleki, mwana wa mdzakazi wake kuti akhale wolamulira anthu a ku Sekemu chifukwa ndi mʼbale wanu. |
6780 | JDG 9:24 | Mulungu anachita zimenezi kuti zoyipa zimene anachitira ana aamuna 70 a Yeru-Baala aja zimubwerere, ndi kuti magazi awo akhale pa Abimeleki mʼbale wawo ndi pa anthu a ku Sekemu amene anamulimbikitsa mtima kuti aphe abale akewo. |
6812 | JDG 9:56 | Mmenemu ndi mmene Mulungu analipsirira tchimo la Abimeleki limene anachitira abambo ake pakupha abale ake 70 aja. |
6885 | JDG 12:14 | Iye anali ndi ana aamuna makumi anayi ndi zidzukulu makumi atatu, amene ankakwera pa abulu 70. Iye anatsogolera Israeli kwa zaka zisanu ndi zitatu. |
7071 | JDG 20:15 | Tsiku limenelo Abenjamini anasonkhanitsa kuchokera ku mizinda yawo ankhondo 26,000 amalupanga awo, osawerengera anthu ena 700 a ku Gibeya amene anasankhidwa. |
7072 | JDG 20:16 | Mwa onsewa panali ankhondo 70 amanzere amene aliyense anali wodziwa kulasa ngakhale tsitsi limodzi ndi mwala osaphonya. |
7103 | JDG 20:47 | Koma anthu 700 anabwerera ndi kuthawira ku chipululu ku thanthwe la Rimoni kumene anakhalako miyezi inayi. |
7352 | 1SA 6:19 | Yehova anakantha amuna a ku Beti-Semesi 70 chifukwa anasuzumira mʼBokosi la Chipangano cha Yehova. Ndipo anzawo analira chifukwa Yehova anawalanga kwambiri. |
7625 | 1SA 17:5 | Iye ankavala chipewa chamkuwa ndi malaya achitsulo olemera makilogalamu 57. |
7882 | 1SA 25:18 | Ndipo Abigayeli sanataye nthawi. Iye anatenga malofu a buledi 200, matumba a chikopa awiri a vinyo, nkhosa zisanu zowotcheratu, makilogalamu 17 a tirigu wokazinga, makeke a mphesa zowuma 100, ndiponso makeke a nkhuyu 200, ndipo anazisenzetsa abulu. |
8216 | 2SA 8:4 | Davide analanda magaleta 1,000, anthu 7,000 okwera magaleta pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha. |
8261 | 2SA 10:18 | Koma iwo anathawa pamaso pa Aisraeli, ndipo Davide anapha anthu okwera pa magaleta 700 ndi ankhondo oyenda pansi 40,000. Davide anaphanso Sobaki mtsogoleri wawo wankhondo ndipo anafera pomwepo. |
8695 | 2SA 23:39 | ndi Uriya Mhiti. Onse pamodzi analipo 37. |
8710 | 2SA 24:15 | Choncho Yehova anabweretsa mliri pa Aisraeli, kuyambira mmawa mpaka pa nthawi imene anafuna mwini wake, ndipo unapha anthu 70,000 kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba. |
8896 | 1KI 5:29 | Solomoni anali ndi anthu amtengatenga 70,000, anthu 80,000 osema miyala ku mapiri, |
8901 | 1KI 6:2 | Nyumba imene Solomoni anamangira Yehova mulitali mwake inali mamita 27, mulifupi mwake inali mamita asanu ndi anayi, ndipo msinkhu wake unali mamita 13 ndi theka. |
9114 | 1KI 11:3 | Iye anali ndi akazi 700 ochokera ku mabanja achifumu ndi azikazi 300 ndipo akaziwo anamusocheretsa. |
9242 | 1KI 14:21 | Rehobowamu mwana wa Solomoni anali mfumu ya ku Yuda. Iye analowa ufumu ali ndi zaka 41, ndipo analamulira zaka 17 ku Yerusalemu, mzinda umene Yehova anawusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti ayikemo Dzina lake. Amayi ake anali Naama, wa ku Amoni. |
9296 | 1KI 16:10 | Zimuri anadzalowa, namukantha ndi kumupha mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda. Ndipo Zimuriyo anakhala mfumu mʼmalo mwake. |
9301 | 1KI 16:15 | Mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda, Zimuri analamulira ku Tiriza masiku asanu ndi awiri. Gulu la ankhondo linali litamanga misasa pafupi ndi Gibetoni, mzinda wa Afilisti. |
9408 | 1KI 19:18 | Komabe ndasunga anthu 7,000 ku Israeli, anthu onse amene mawondo awo sanagwadirepo Baala, onse amene pakamwa pawo sipanapsompsoneko fano lake.” |
9426 | 1KI 20:15 | Choncho Ahabu anawerenga asilikali achinyamata a nduna za mʼzigawo ndipo onse analipo 232. Ndipo anawerenganso ankhondo a ku Israeli ndipo onse analipo 7,000. |
9441 | 1KI 20:30 | Ena onse otsala anathawira ku Afeki, kumene khoma linagwera anthu 27,000. Ndipo Beni-Hadadi anathawira mu mzinda, nakabisala mʼchipinda chamʼkati. |
9535 | 1KI 22:52 | Ahaziya mwana wa Ahabu anakhala mfumu ya ku Israeli ku Samariya mʼchaka cha 17 cha Yehosafati mfumu ya ku Yuda, ndipo analamulira Israeli zaka ziwiri. |
9606 | 2KI 3:26 | Mfumu ya ku Mowabu itaona kuti nkhondo ikumulaka, inatenga anthu 700 a malupanga kuti athawe modutsa mfumu ya ku Edomu, koma inalephera. |
9798 | 2KI 10:1 | Tsono Ahabu anali ndi ana aamuna 70 a ku Samariya. Ndipo Yehu analemba makalata nawatumiza ku Samariya kwa atsogoleri a mu mzinda wa Yezireeli, kwa akuluakulu ndiponso kwa amene ankalera ana a Ahabu, nati, |
9803 | 2KI 10:6 | Ndipo Yehu anawalembera kalata yachiwiri yonena kuti, “Ngati inu muli mbali yanga ndi kuti mudzandimvera, mudule mitu ya ana a mbuye wanu ndipo mubwere nayo kwa ine ku Yezireeli mawa nthawi ngati yomwe ino.” Tsono ana a mfumu onse 70 anali pamodzi ndi akuluakulu a mu mzindamo, amene ankawalera. |
9804 | 2KI 10:7 | Kalatayo itafika, anthuwo anatenga ana a mfumu 70 aja ndi kuwapha onse. Anayika mitu yawo mʼmadengu ndi kuyitumiza ku Yezireeli kwa Yehu. |
9876 | 2KI 13:1 | Mʼchaka cha 23 cha ufumu wa Yowasi mwana wa Ahaziya mfumu ya Yuda, Yehowahazi, mwana wa Yehu anakhala mfumu ya Israeli mu Samariya, ndipo analamulira zaka 17. |
9885 | 2KI 13:10 | Mʼchaka cha 37 cha Yowasi mfumu ya Yuda, Yehowahazi anakhala mfumu ya Israeli mu Samariya, ndipo analamulira zaka 16. |
9930 | 2KI 15:1 | Mʼchaka cha 27 cha Yeroboamu mfumu ya Israeli, Azariya mwana wa Amaziya mfumu ya Yuda anayamba kulamulira. |
9968 | 2KI 16:1 | Mʼchaka cha 17 cha Peka mwana wa Remaliya, Ahazi mwana wa Yotamu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira. |
10222 | 2KI 24:16 | Mfumu ya Babuloni inatumizanso ku Babuloni anthu ankhondo 70,000, anthu amphamvu ndi okonzeka kupita ku nkhondo, anthu aluso ndi amisiri osula 1,000. |
10253 | 2KI 25:27 | Pa chaka cha 37 cha ukapolo wa Yehoyakini mfumu ya Yuda, chaka chimene Evili-Merodaki anakhala mfumu ya Babuloni, anamasula Yehoyakini mʼndende pa mwezi wa 12 pa tsiku la 27. |
10450 | 1CH 5:18 | Mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la Manase, anali ndi anthu 44, 760 okonzeka kulowa usilikali; anthu amatupi amphamvu, amene amatha kugwiritsa ntchito chishango ndi lupanga, amene amatha kugwiritsa ntchito uta, amene anaphunzitsidwa kumenya nkhondo. |
10544 | 1CH 7:5 | Abale awo onse a mʼbanja la Isakara amene anali odziwa kumenya nkhondo analipo 87,000, olembedwa potsata mibado yawo. |
10550 | 1CH 7:11 | Ana onsewa a Yediaeli anali atsogoleri a mabanja. Analipo anthu 17,200 amene anali okonzeka kupita ku nkhondo. |
10632 | 1CH 9:13 | Ansembe amene anali atsogoleri a mabanja awo analipo 1,760. Anali anthu amphamvu ndi odziwa kutumikira mʼnyumba ya Mulungu. |
10750 | 1CH 12:26 | Anthu a fuko la Simeoni, asilikali okonzekera nkhondo analipo 7,100; |
10752 | 1CH 12:28 | mtsogoleri Yehoyada wa banja la Aaroni anabweranso ndi anthu 3,700, |
10759 | 1CH 12:35 | Anthu a fuko la Nafutali, analipo atsogoleri 1,000 pamodzi ndi anthu 37,000 onyamula zishango ndi mikondo; |
10899 | 1CH 18:4 | Davide analanda magaleta 1,000, anthu okwera magaleta 7,000 pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha. |
10930 | 1CH 19:18 | Koma iwo anathawa pamaso pa Aisraeli, ndipo Davide anapha anthu okwera pa magaleta 7,000 ndi ankhondo oyenda pansi 40,000. Iye anaphanso Sofaki, mtsogoleri wawo wankhondo. |
10944 | 1CH 21:5 | Yowabu anapereka chiwerengero cha anthu ankhondo kwa Davide: Mu Israeli monse munali anthu ankhondo 1,100,000 amene amadziwa kugwiritsa ntchito lupanga, kuphatikizapo anthu 470,000 a fuko la Yuda. |
10953 | 1CH 21:14 | Choncho Yehova anabweretsa mliri pa Aisraeli, ndipo unapha Aisraeli 70,000. |
11035 | 1CH 24:15 | a 17 anagwera Heziri, a 18 anagwera Hapizezi, |